Tikule mu uzimu

Tikule mu uzimu KOD MUNAMULANDILA YESU KHRISTU???

07/04/2026

the eagles choice choir mchezi living waters ���

palibe chomulaka ambuye
05/04/2026

palibe chomulaka ambuye

02/03/2026

The eagles voice choir mchezi living waters church
tittle sikwabwino kuno bola kumwamba

26/02/2026

Big shout out to my newest top fans! Kho Dada, Phio Dolla, Florence Limbani, Mercy Ngongondole, Weston Makwakwa, Mphatso Longwe, Chisomo Wa Namakupula, Rabecca Mchemo, Mwana Wa Msade Tondo, Grace Majiga, Towera Golah Mwanza, Fadile Chima, Fatsani Kalima, Ãlëx Sïlîyâ, Chifuniro Nkhoma, Tapiwa Chiwaya, Lastnumber No-one Behind, Jane Bernardo, Binalison Saukan, Brilliant Gilb Nkhoma

29/01/2026

TANGOOTCHANI MTENGOWO BASI

Mmudzi wina munamveka mau ak*ti njoka🗣, njoka🗣, ndipo anthu onse anathamanga ndizida mmanja k*ti akaphe njokayo.
Azimai anatenga misi, azibambo anatenga zikwanje, mauta ena zibonga k*ti akaphe njokayo.

Chinali chinjoka chachikulu🐍, koma chitaona anthu, icho chinathawira mu mphanga ya mtengo omwe unali pafupi kwambiri ndinyumba ya amfumu 🌳🏠. Anthu anayesetsa k*ti aiphe koma zinalephera.

Amfumu atamva izi anakana k*ti chilombocho achisiye chilindimoyo mumtengo omwe ulipakhomo pawo, ndipo analamula k*ti mtengowo uwotchedwe 🔥 ndipo zinachitikadi.

🥦FUNSO🥦?
Unalakwanji mtengo k*ti uwotchedwe🤷‍♀?
Ngati mukuganiza k*ti nchifukwa choti unasunga mphanga yomwe munalowa njoka🐍, zikomo kwambiri.

🥦PHUNZIRO🥦.
Njoka ndiye satana, mtengo ndife wanthu ndipo mphanga ndiwo mtima wathu, pamene mfumu ndiye Mulungu.

Tikuyenera kusamala kwambiri, chifukwa tikampatsa satana kulowa mumtima mwathu ife tidzaonongedwa monga zinakhalira ndi mtengo uja. Cholinga cha Mulungu ndikudzaononga tchimo padziko lino lapansi, koma tikalisunga tchimolo mumtima mwathu, ndithu tidzaonongedwa mwai opulumuka ulimmanja mwathu

Ambuye Akudalitseni Nonse Mukhale Ndi Tsiku lopambana AMEN 🙏. Tikule mu uzimu

22/12/2025

Nthawi Zina Mamuna ukhoza kumakumana ndi matsoka pamoyo wako chifkwa Cha nkazi amene umukwatira

Ukhoza kumakhala wekha kma nkumakhala ndimwai wandalama ntchito osamasowa kma kungokwatira chilichonse kusokonekela chifkwa cha mntundu wa munthu amene unakwatilana naye

2 Samueli : 11 : 13-15
13. Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14. Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15. Mʼkalatayo analembamo k*ti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha k*ti akanthidwe ndi kufa.

Olendo omaliza wa Uria kupta kukamenya nkhondo ngakhale mwini wakeyoso ankadabwa KT lero lokha lokha zakhala anthu sakundileletsa osadziwa nkhondo imeneyo ikuchokela Beteseba 😥

Uria akanapta kukagona ndi Beteseba ndiye KT Beteseba sakanamuuza Uria KT wanyengana ndi Davide

Mulizinsinsi Zina mmabanjamu zomwe zikupangitsa anthu awirinu KT wina azimva kuwawa,achulukilenji lero aBeteseba omasunga ndalama paokha mmabanja

Mulungu atithandize kukupatsani nkazi yemwe azabweletse Zisomo pamoyo wanu akazi Ena amakhala mdalitso pomwe Ena amabweletsa matsoka

M'banja mukazangoyamba kusungilana zinsinsi zinthu zimasokonekela alelluyah

Ana Amulungu tidziwe k*ti;Nthawi zina Chauta amatha kulimbitsa nyengo pa Moyo wa Munthu, sichifukwa choti munthuyo ngosa...
03/12/2025

Ana Amulungu tidziwe k*ti;
Nthawi zina Chauta amatha kulimbitsa nyengo pa Moyo wa Munthu, sichifukwa choti munthuyo ngosafunikira ayi, koma k*ti Mulungu akalemekedzekedwe,,,, Amen 👏

Chimodzimodz apa tikuona k*ti Mulungu akulimbitsa dala mtima wa Faraoh k*ti Aigupto adziwalondorabe a Israel ndicholinga chot pakuona Mulungu akuwamenyera Nkhondo Israel akalemekedzekedwe👏
amen 🙏🙏

Tanvani nkhaniyi 😭😭😭😭🗣️🙏🙏Padali mnyamata🙍‍♂️ wina  wa zaka 18 pa Sukulu ina  mdera la kwawo.Mnyamatayi🙍‍♂️ anali olimbik...
29/11/2025

Tanvani nkhaniyi 😭😭😭😭🗣️🙏🙏Padali mnyamata🙍‍♂️ wina wa zaka 18 pa Sukulu ina mdera la kwawo.
Mnyamatayi🙍‍♂️ anali olimbikila class👨‍🏫 ndipo amakhoza mopasa chidwi zedi.
Aliyense amazizwa🤔 ndi kakhozedwe ka mwanayi ngakhale aphunzitsi anali kumuyamikila.
Mpikitsano ulionse iye amakhala owina chifukwa cha nzeru zakezi.
Mphoto zosiyanasiyana anali k*tenga ndi iye.

Ndipo nthawi inafika nalemba mayeso ake a Form 4 napita kunyumba kukadikila zotsatila....
Sukulu pamodzi ndi a head Chiyembekezo chake chonse chinali pa mnyamatayi k*ti akhala oyamba kupita Ku University.

Koma zinali zonvesa chisoni koma zosanveseseka k*tasala matsiku atatu k*ti mayeso atuluke mnyamatayi anadwala kwa nthawi yochepa namwalira⚰️😭😭😭.
Ndipo zotsatila zitabwera mnyamatayi anakhoza 9 points kuposa anzake onse.
Komatu zotsatila izi zinabwera mnyamatayi atamwalira⚰️😭😭 maphunziro ake adakhala opanda mphindu.

Imfa sinaone k*ti mwanayi wavutika motani k*ti afike apa😭😭,Ukuwerengawe dziwa k*ti ulipamenepo ndimoyo ndicholinga osati chifukwa choti ndiwe opambana.Analipi amzeru ,achuma pano alik*ti⁉️Azako unabadwa nawo anamwalira koma iwe ulindimoyobe.Mulungu odziwa kusunga akusunge iwe ndiapabanjalako kufikana cholinga chake paiwe chizakwanilitsidwe, AMBUYE 🙏 zikomo chifukwa chamoyo wanga AMEN🙏

Chonde kwa 1 minitsi yokha MULUNGU akudalitsani mukapanga follow 👇 k*ti tikhalire limodzi 🙏.tikule mu uzimu 🙏

16/11/2025

Tikule mu uzimu
Momwe Mwagwilira Phone Yanu Kuti Isagwe
Ndimomweso Yehova Wasungira Moyo Wanu
😭😭😭😭😭 1 Min Thank You God🙏🙏sindisiya kulira mpaka ulembe k*t Amen 😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭😭
Tikule mu uzimumu uzimu

Address

1882AA
Lilongwe

Telephone

+265995455277

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Tikule mu uzimu posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share