26/05/2026
Kutsatira kupezeka kwa khanda lomwe linatayidwa m'dera la mfumu yaikulu Chidzuma m'boma la Kasungu, mayi wina waku Area 36, mu mzinda wa Lilongwe, wati khandali ndi lake ponena kuti linachita kubedwa.
Mkulu woona za chisamaliro cha anthu m'bomali, a Ephraim Njikho, wati mayiyu anafikadi ku ofesi kwawo, koma kaamba koti palibe umboni wotsimikizika kuti khandali ndi lake, akana kupereka khandali.
Mmawu ake, wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi m'bomali, a Miracle Hauli, watsimikiza za nkhaniyi ponena kuti ngakhale mayiyu anakakamila kufuna kutenga mwanayu komabe iye akufunsidwa kaye mafunso omwe athandizire kafukufuku opeza mwini wake wa khandali.
Full video ili mu comment 👇